Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 24:5-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. ndipo m'mene anakhala ndi mantha naweramira pansi nkhope zao, anati kwa iwo, Mufuniranji wamoyo pa akufa?

6. Palibe kuno iye, komatu anauka; kumbukilani muja adalankhula nanu, pamene analinso m'Galileya,

7. ndi kunena, kuti, Mwana wa munthu ayenera kuperekedwa m'manja a anthu ocimwa, ndi kupacikidwa pamtanda, ndi kuuka tsiku lacitatu.

8. Ndipo anakumbukila mau ace, nabwera kucokera kumanda,

9. nafotokozera zonse khumi ndi mmodziwo, ndi otsala onse omwe.

10. Koma panali Mariya wa Magadala, ndi Y ohana, ndi Mariya amace wa Yakobo, ndi akazi ena pamodzi nao amene ananena izi kwa atumwiwo.

11. Ndipo mau awa anaoneka pamaso pao ngati nkhani zacabe, ndipo sanamvera akaziwo.

12. Koma Petro ananyamuka nathamangira kumanda, ndipo powerama anaona nsaru zoyera pa zokha; ndipo anacoka nanka kwao, nazizwa ndi cija cidacitikaco.

13. Ndipo taonani, awiri a mwa iwo analikupita tsiku lomwelo kumudzi dzina lace Emau, wosiyana ndi Yerusalemu mastadiya makumi asanu ndi limodzi.

14. Ndipo iwowa anakambirana nkhani za izi zonse zidacitika.

15. Ndipo kunali m'kukambirana kwao ndi kufunsana, Yesu mwini anayandikira, natsagana nao.

16. Koma maso ao anagwidwa kuti asamzindikire iye.

17. Ndipo anati kwa iwo, Mau awa ndi otani mulandizanawo poyendayenda? Ndipo anaima ndi nkhope zao zacisoni.

18. Ndipo mmodzi wa iwo, dzina lace Kleopa, anayankha nati kwa iye, Kodi iwe wekha ndiwe mlendo m'Yerusalemu ndi wosazindikira zidacitikazi masiku omwe ano?

19. Ndipo anati kwa iwo, Zinthu zanji? Ndipo anati kwa iye, lzi za Yesu Mnazarene, ndiye munthu mneneri wamphamvu m'nchito, ndi m'mau, pamaso pa Mulungu ndi anthu onse;

20. ndikuti ansembe akulu ndi akulu athu anampereka iye ku ciweruziro ca imfa, nampacika iye pamtanda.

21. Ndipo tinayembekeza ife kuti iye ndiye wakudzayo kudzaombola Israyeli, Komatunso, pamodzi ndi izi zonse lero ndilo tsiku lacitatu kuyambira zidacitika izi.

22. Komatu akazi enanso a mwa ife anatidabwitsa, ndiwo amene analawirira kumanda;

23. ndipo m'mene sanapeza mtembo wace, anadza, nanena kuti adaona m'masomphenya angelo, amene ananena kuti ali ndi moyo iye.

Werengani mutu wathunthu Luka 24