Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 24:39-51 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Penyani manja anga ndi mapazianga, kuti Ine ndine mwini: 2 ndikhudzeni, ndipo penyani; pakuti mzimu ulibe, mnofu ndi mafupa, monga muona ndirinazo Ine.

40. Ndipo m'mene ananena ici, anawaonetsera iwo manja ace ndi mapazi ace.

41. Koma pokhala iwo cikhalire osakhulupirira cifukwa ca cimwemwe, nalikuzizwa, anati kwa iwo, 3 Muli nako kanthu kakudya kuno?

42. Ndipo anampatsa iye cidutsu ca nsomba yokazinga.

43. Ndipo 4 anacitenga, nacidya pamaso pao.

44. Ndipo anati kwa iwo, 5 Awa ndi mauwo ndinalankhula nanu, paja ndinakhala ndi inu, kuti ziyenera kukwanitsidwa zonse zolembedwa za Ine m'cilamulo ca 6 Mose, ndi aneneri, ndi masalmo.

45. Ndipo 7 anawatsegulira mitima yao, kuti adziwitse malembo;

46. ndipo anati kwa iwo, 8 Kotero kwalembedwa, kuti Kristu amve zowawa, nauke kwa akufa tsiku lacitatu;

47. ndi kuti kulalikidwe m'dzina lace kulapa ndi 9 kukhululukidwa kwa macimo kwa 10 mitundu yonse, kuyambira ku Yerusalemu.

48. 11 Inu ndinu mboni za izi.

49. Ndipo onani, 12 Ine nditumiza pa inu lonjezano la Atate wanga; koma khalani inu m'mudzi muno, kufikira mwabvekedwa ndi mphamvu yocokera Kumwamba.

50. Ndipo anaturuka nao kufikira ku Betaniya; nakweza manja ace, nawadalitsa.

51. Ndipo kunali, 13 pakuwadalitsa iye analekana nao, natengedwa kunka Kumwamba.

Werengani mutu wathunthu Luka 24