Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 24:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo anati kwa iwo, Zinthu zanji? Ndipo anati kwa iye, lzi za Yesu Mnazarene, ndiye munthu mneneri wamphamvu m'nchito, ndi m'mau, pamaso pa Mulungu ndi anthu onse;

20. ndikuti ansembe akulu ndi akulu athu anampereka iye ku ciweruziro ca imfa, nampacika iye pamtanda.

21. Ndipo tinayembekeza ife kuti iye ndiye wakudzayo kudzaombola Israyeli, Komatunso, pamodzi ndi izi zonse lero ndilo tsiku lacitatu kuyambira zidacitika izi.

22. Komatu akazi enanso a mwa ife anatidabwitsa, ndiwo amene analawirira kumanda;

Werengani mutu wathunthu Luka 24