Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 24:18-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo mmodzi wa iwo, dzina lace Kleopa, anayankha nati kwa iye, Kodi iwe wekha ndiwe mlendo m'Yerusalemu ndi wosazindikira zidacitikazi masiku omwe ano?

19. Ndipo anati kwa iwo, Zinthu zanji? Ndipo anati kwa iye, lzi za Yesu Mnazarene, ndiye munthu mneneri wamphamvu m'nchito, ndi m'mau, pamaso pa Mulungu ndi anthu onse;

20. ndikuti ansembe akulu ndi akulu athu anampereka iye ku ciweruziro ca imfa, nampacika iye pamtanda.

21. Ndipo tinayembekeza ife kuti iye ndiye wakudzayo kudzaombola Israyeli, Komatunso, pamodzi ndi izi zonse lero ndilo tsiku lacitatu kuyambira zidacitika izi.

22. Komatu akazi enanso a mwa ife anatidabwitsa, ndiwo amene analawirira kumanda;

23. ndipo m'mene sanapeza mtembo wace, anadza, nanena kuti adaona m'masomphenya angelo, amene ananena kuti ali ndi moyo iye.

24. Ndipo ena a iwo anali nafe anacoka kunka kumanda, napeza monga momwe akazi adanena; koma Iyeyo sanamuona.

25. Ndipo iye anati kwa iwo, Opusa inu, ndiozengereza mtima kusakhulupirira zonse adazilankhula aneneri!

26. Kodi sanayenera Kristu kumva zowawa izi, ndi kulowa ulemerero wace?

27. Ndipo anayamba kwa Mose, ndi kwa aneneri onse, nawatanthauzira iwo m'malembo onse zinthu za iye yekha.

28. Ndipo anayandikira ku mudzi umene analikupitako; ndipo anacita ngati anafuna kupitirira.

29. Ndipo anamuumiriza iye, nati, Khalani ndi ife; pakuti kuli madzulo, ndipo dzuwa lapendekatu, Ndipo analowa kukhala nao.

30. Ndipo kunali m'mene iye anaseama nao pacakudya, anatenga mkate, naudalitsa naunyema, napatsa iwo.

31. Ndipo maso ao anatseguka, ndipo anamzindikira iye; ndipo anawakanganukira iye, nawacokera.

32. Ndipo anati wina kwa mnzace, Mtima wathu sunali wotentha m'kati mwathu nanga m'mene analankhula nafe m'njira, m'mene anatitseguliramalembo?

33. Ndipo ananyamuka nthawi yomweyo nabwera ku Yerusalemu, napeza khumi ndi mmodziwo, ndi iwo anali nao atasonkhana pamodzi,

34. nanena, Ambuye anauka ndithu, naonekera kwa Simoni.

35. Ndipo iwo anawafotokozera za m'njira, ndi umo anadziwika nao m'kunyema kwa mkate.

36. Ndipo pakulankhula izi iwowa, iye anaimirira pakati pao; nanena nao, Mtendere ukhale nanu.

37. Koma anaopsedwandi kucita mantha, 1 nayesa alikuona mzimu.

Werengani mutu wathunthu Luka 24