Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 24:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo iwowa anakambirana nkhani za izi zonse zidacitika.

15. Ndipo kunali m'kukambirana kwao ndi kufunsana, Yesu mwini anayandikira, natsagana nao.

16. Koma maso ao anagwidwa kuti asamzindikire iye.

17. Ndipo anati kwa iwo, Mau awa ndi otani mulandizanawo poyendayenda? Ndipo anaima ndi nkhope zao zacisoni.

18. Ndipo mmodzi wa iwo, dzina lace Kleopa, anayankha nati kwa iye, Kodi iwe wekha ndiwe mlendo m'Yerusalemu ndi wosazindikira zidacitikazi masiku omwe ano?

19. Ndipo anati kwa iwo, Zinthu zanji? Ndipo anati kwa iye, lzi za Yesu Mnazarene, ndiye munthu mneneri wamphamvu m'nchito, ndi m'mau, pamaso pa Mulungu ndi anthu onse;

Werengani mutu wathunthu Luka 24