Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 23:35-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Ndipo anthu anaima alikupenya, Ndi akurunso anamlalatira iye nanena, Anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati iye ndiye Kristu wa Mulungu, wosankhidwa wace.

36. Ndipo asilikarinso anamnyoza, nadza kwa iye, nampatsa vinyo wosasa,

37. nanena, Ngati Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda, udzipulumutse wekha.

38. Ndipo kunalinso lembo pamwamba pace, ndilo: UYU NDIYE MFUMU YAAYUDA.

39. Ndipo mmodzi wa ocita zoipa anapacikidwawo anamcitira iye mwano nanena, Kodi suli Kristu Iwe? udzipulumutse wekha ndi ife.

40. Koma winayo anayankha, namdzudzula iye, nati, Kodi suopa Mulungu, poona uli m'kulangika komweku?

41. Ndipo ifetu kuyenera; pakuti tirikulandira zoyenera zimene tinazicita: koma munthu uyu sanacita kanthu kolakwa.

42. Ndipo ananena, Yesu, ndikumbukileni m'mene mulowa Ufumuwanu.

Werengani mutu wathunthu Luka 23