Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 23:34-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Ndipo Yesu ananena, Atate, muwakhululukire iwo, pakuti sadziwa cimene acita. Ndipo anagawana zobvala zace, poyesa maere.

35. Ndipo anthu anaima alikupenya, Ndi akurunso anamlalatira iye nanena, Anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati iye ndiye Kristu wa Mulungu, wosankhidwa wace.

36. Ndipo asilikarinso anamnyoza, nadza kwa iye, nampatsa vinyo wosasa,

37. nanena, Ngati Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda, udzipulumutse wekha.

38. Ndipo kunalinso lembo pamwamba pace, ndilo: UYU NDIYE MFUMU YAAYUDA.

39. Ndipo mmodzi wa ocita zoipa anapacikidwawo anamcitira iye mwano nanena, Kodi suli Kristu Iwe? udzipulumutse wekha ndi ife.

40. Koma winayo anayankha, namdzudzula iye, nati, Kodi suopa Mulungu, poona uli m'kulangika komweku?

Werengani mutu wathunthu Luka 23