Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 20:8-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ndingakhale Inenso sindikuuzani ulamuliro umene ndicita nao zinthu izi.

9. Ndipo iye anayamba kunena kwa anthu fanizo ili: Munthu analima munda wamphesa, naukongoletsa kwa olima munda, nanka ku dziko lina, nagonerako nthawi yaikuru.

10. Ndipo pa nyengo ya zipatso anatumiza kapolo wace kwa olima mundawo, kuti ampatseko cipatso ca mundawo; koma olimawo anampanda, nambweza wopanda kanthu.

11. Ndipo anatumizanso kapolo wina; ndipo iyenso anampanda, namcitira cipongwe, nambweza, wopanda kanthu.

12. Ndipo anatumizanso wina wacitatu; ndipo iyenso anamlasa, namtaya kunja.

13. Ndipo mwini mundawo anati, Ndidzacita ciani? Ndidzatuma mwana wanga amene ndikondana naye; kapena akamcitira iye ulemu.

14. Koma olimawo, pamene anamuona, anauzana wina ndi mnzace, nati, Uyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe, kuti colowa cace cikhale cathu.

15. Ndipo anamponya kunja kwa mundawo, namupha, Pamenepo mwini munda wamphesawo adzawacitira ciani?

16. iye adzafika nadzaononga olima munda aja, nadzapatsa munda kwa ena. Ndipo pamene iwo anamva, anati, Musatero iail

17. Koma iye anawapenyetsa iwo, nati, Nciani ici cinalembedwa,Mwala umene anaukana omanga nyumba,Womwewu unakhala mutu wa pangondya.

18. Munthu yense wakugwa pa mwala uwu, adzaphwanyika; koma iye amene udzamgwera, udzamupha.

19. Ndipo alembi ndi ansembe akuru anafunafuna kumgwira ndi manja nthawi yomweyo; ndipo anaopa anthu; pakuti anazindikira kuti ananenera pa iwo fanizo ili.

20. Ndipo anamyang'anira, natumiza ozonda, amene anadzionetsera ngati olungama mtima, kuti akamkole pa mau ace, kotero kuti akampereke iye ku ukulu ndi ulamuliro wa kazembe.

Werengani mutu wathunthu Luka 20