44. koma iwo anayesa kuti iye ali m'cipiringu ca ulendo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi; ndipo anayamba kumfunafuna iye mwa abale ao ndi mwa anansi ao;
45. ndipo pamene sanampeza, anabwera ku Yerusalemu, namfunafuna iye.
46. Ndipo pakupita masiku atatu, anampeza iye m'Kacisi, analikukhala pakati pa aphunzitsi, namva iwo, nawafunsanso mafunso.
47. Ndipo 4 onse amene anamva iye anadabwa ndi cidziwitso cace, ndi mayankho ace.