Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 2:41-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Ndipo atate wace ndi amace 3 akamuka caka ndi caka ku Yerusalemu ku Paskha.

42. Ndipo pamene iye anakhala ndi zaka zace khumi ndi ziwiri, anakwera iwo monga macitidwe a phwando;

43. ndipo pakumariza masiku ace, pakubwera iw, mnyamatayo Yesu anatsala m'mbuyo ku Yerusalemu. Ndipo atate ndi amace sanadziwa;

44. koma iwo anayesa kuti iye ali m'cipiringu ca ulendo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi; ndipo anayamba kumfunafuna iye mwa abale ao ndi mwa anansi ao;

45. ndipo pamene sanampeza, anabwera ku Yerusalemu, namfunafuna iye.

46. Ndipo pakupita masiku atatu, anampeza iye m'Kacisi, analikukhala pakati pa aphunzitsi, namva iwo, nawafunsanso mafunso.

47. Ndipo 4 onse amene anamva iye anadabwa ndi cidziwitso cace, ndi mayankho ace.

Werengani mutu wathunthu Luka 2