Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 2:35-52 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. eya, ndipo lupanga lidzakupyoza iwe moyo wako; kuti maganizo a m'mitima yambiri akaululidwe.

36. Ndipo panali Anna, mneneri wamkazi, mwana wa Fanueli, wa pfuko la Aseri; amene anali wokalamba ndithu, nakhala ndi mwamuna wace, kuyambira pa unamwali wace,

37. zaka zisanu ndi ziwiri, ndipo anali wamasiye wa kufikira zaka zace: makumi asanu ndi atatu mphambu zinai, amene sanacoka kuKacisi, wotumikira Mulungu ndi kusala kudya ndi kupemphera usiku ndi usana.

38. Ndipo iye anafikako pa nthawi yomweyo, nabvomerezanso kutama Mulungu, nalankhula za iye kwa anthu onse 1 akuyembekeza ciombolo ca Yerusalemu.

39. Ndipo pamene iwo anatha zonse monga mwa cilamulo ca Ambuye, anabwera ku Galileya, ku mudzi kwao, ku Nazarete.

40. Ndipo 2 mwanayo anakula nalimbika, nalikudzala ndi nzeru; ndi cisomo ca Mulungu cinali pa iye.

41. Ndipo atate wace ndi amace 3 akamuka caka ndi caka ku Yerusalemu ku Paskha.

42. Ndipo pamene iye anakhala ndi zaka zace khumi ndi ziwiri, anakwera iwo monga macitidwe a phwando;

43. ndipo pakumariza masiku ace, pakubwera iw, mnyamatayo Yesu anatsala m'mbuyo ku Yerusalemu. Ndipo atate ndi amace sanadziwa;

44. koma iwo anayesa kuti iye ali m'cipiringu ca ulendo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi; ndipo anayamba kumfunafuna iye mwa abale ao ndi mwa anansi ao;

45. ndipo pamene sanampeza, anabwera ku Yerusalemu, namfunafuna iye.

46. Ndipo pakupita masiku atatu, anampeza iye m'Kacisi, analikukhala pakati pa aphunzitsi, namva iwo, nawafunsanso mafunso.

47. Ndipo 4 onse amene anamva iye anadabwa ndi cidziwitso cace, ndi mayankho ace.

48. Ndipo m'mene anamuona iye, anadabwa; ndipo amace anati kwa iye, Mwanawe, wacitiranji ife cotero; taona, atate wako ndi ine tinalikufunafuna Iwe ndi kuda nkhawa.

49. Ndipo iye anati kwa iwo, Kuli bwanji kuti munalikundifunafuna Ine? Simunadziwa kodi kuti kundiyenera Ine 5 ndikhale m'zace za Atate wanga?

50. Ndipo 6 sanadziwitsa mau amene iye analankhula nao.

51. Ndipo anatsika nao pamodzi nadza ku Nazarete; nawamvera iwo: ndipo 7 amace anasunga zinthu izi zonse mumtima mwace.

52. Ndipo Yesu 8 anakulabe m'nzeru ndi mumsinkhu, ndi m'cisomo ca pa Mulungu ndi ca pa anthu.

Werengani mutu wathunthu Luka 2