Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 19:4-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo anathamanga, natsogola, nakwera mumkuyu kukamuona iye; pakuti anati apite njira yomweyi.

5. Ndipo m'mene anadza pamalopo Yesu anakweza maso nati kwa iye, Zakeyu, fulumira, nutsike; pakuti lero ndiyenera kukhala m'nyumba mwako.

6. Ndipo anafulumira, natsika, namlandira iye wokondwera.

7. Ndipo m'mene anaciona anadandaula onse, nanena, Analowa amcereze munthu ali wocimwa.

8. Ndipo Zakeyu anaimirira nati kwa Ambuye, Taonani, Ambuye, gawo limodzi la zanga zonse zogawika pakati ndipatsa osauka; ndipo ngati ndalanda kanthu kwa munthu monyenga, ndimbwezera kanai.

9. Ndipo Yesu anati kwa iye, Lero cipulumutso cagwera nyumba iyi, popeza iyenso ndiye mwana wa Abrahamu.

10. Pakuti Mwana wa munthu anadza kufunafuna ndi kupulumutsa, cotayikaco.

11. Ndipo pakumva izi iwo, iye anaonjeza nanena fanizo, cifukwa anali iye pafupi pa Yerusalemu, ndipo iwo anayesa kuti Ufumu wa Mulungu ukuti uonekere pomwepo.

12. Pamenepo: anati, Munthu wa pfuko lomveka ananka ku dziko lakutali, kudzilandirira yekha ufumu, ndi kubwerako.

13. Ndipo anaitana akapolo ace khumi, nawapatsa iwo ndalama khumi, nati kwa iwo, Cita nazoni malonda kufikira ndibweranso.

14. Koma mfulu za pamudzi pace zinamuda, nizituma akazembe amtsate m'mbuyo ndi kunena, Ife sitifuna munthuyu akhale mfumu yathu.

15. Ndipo kunali, pakubwera iye, atalandira ufumuwo, anati aitanidwe kwa iye akapolo aja, amene adawapatsa ndalamazo, kuti adziwe umo anapindulira pocita malonda.

Werengani mutu wathunthu Luka 19