Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 16:10-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Iye amene akhulupirika m'cacing'onong'ono alinso wokhulupirika m'cacikuru; ndipo iye amene ali wosalungama m'cacing'onong'ono alinso wosalungama m'cacikuru.

11. Cifukwa cace ngati simunakhala okhulupirika m'cuma ca cosalungama, adzakhulupirira inu ndani ndi cuma coona?

12. Ndipo ngati simunakhala okhulupirika ndi zace za wina, adzakupatsani inu ndani za inu eni?

13. Palibe mnyamata wa m'nyumba akhoza kukhala kapolo wa ambuye awiri; pakuti kapena adzamuda wina, nadzakonda winayo; kapena adzatsata wina, nadzapeputsa winayo. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa Cuma.

14. Koma Marisi, ndiwo okonda ndalama, anamva izi zonse; ndipo anamseka.

15. Ndipo anati kwa iwo, Inu ndinu odziyesera nokha olungama pamaso pa anthu; koma Mulungu azindikira mitima yanu; cifukwa ici cimene cikuzika mwa anthu ciri conyansa pamaso pa Mulungu.

16. Cilamulo ndi aneneci analipo kufikira pa Yohane; kuyambira pamenepo ulalikidwa Uthenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu, ndipo munthu ali yense akangamira kulowamo.

17. Kuti kumwamba ndi dziko lapansi zicoke nkwapafupi, koma kuti kalembo kakang'ono ka cilamulo kagwe nkwapatali.

18. Yense wakusudzula mkazi wace, nakwatira wina, acita cigololo; ndipo iye amene akwatira wosudzulidwayo, acita cigololo,

Werengani mutu wathunthu Luka 16