Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 15:6-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo pakufika kunyumba kwace amema abwenzi ace ndi anansi ace, nanena nao, Kondwerani ndi ine, cifukwa ndinapeza nkhosa yanga yotayikayo.

7. Ndinena kwa inu, kotero kudzakhala cimwemwe Kumwamba cifukwa ca wocimwa mmodzi wotembenuka mtima, koposa anthu olungama makumi asanu ndi anai mphambu asanu ndi anai, amene alibe kusowa kutembenuka mtima.

8. Kapena mkazi wanji ali nazo ndalama zasiliva khumi, ngati itayika imodzi, sayatsa nyali, nasesa m'nyumba yace, nafunafuna cisamalire kufikira akaipeza?

9. Ndipo m'mene aipeza amema abwenzi ace ndi anansi ace, nanena; Kondwerani ndi ine, cifukwa ndinapeza ndalama ndidatayayo.

10. Comweco, ndinena kwa inu, kuli cimwemwe pamaso pa angelo a Mulungu cifukwa ca munthu wocimwa mmodzi amene atembenuka mtima.

11. Ndipo iye anati, Munthu wina anali ndi ana amuna awiri;

12. ndipo wamng'onoyo anati kwa atate wace, Atate, ndigawirenitu zanga za pa cuma canu. Ndipo iye anawagawira za moyo wace.

13. Ndipo pakupita masiku owerengekamwana wamng'onoyo anasonkhanitsa zonse, napita ulendo wace ku dziko lakutari; ndipo komweko anamwaza cuma cace ndi makhalidwe a citayiko.

14. Ndipo pamene anatha zace zonse, panakhala njala yaikuru m'dziko muja, ndipo iye anayamba kusowa.

15. Ndipo anamuka nadziphatikiza kwa mfulu imodzi ya dziko lija; ndipo uyu anamtumiza kubusa kwace kukaweta nkhumba.

Werengani mutu wathunthu Luka 15