Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 15:19-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. sindiyeneranso konse kuchulidwa mwana wanu; mundiyese ine ngati mmodzi wa anchito anu.

20. Ndipo iye ananyamuka, nadza kwa atate wace. Koma pakudza iye kutali, atate wace anamuona, nagwidwa cifundo, nathamanga, namkupatira pakhosi pace, nampsompsonetsa.

21. Ndipo mwanayo anati kwa iye, Atate ndinacimwira Kumwamba ndi pamaso panu, sindiyeneranso konse kuchulidwa mwana wanu.

22. Koma atateyo ananena kwaakapolo ace, Turutsani msanga mwinjiro wokometsetsa, nimumbveke; ndipo mpatseni phete ku dzanja lace ndi nsapato ku apazi ace;

23. ndipo idzani naye mwana wa ng'ombe wonenepa, mumuphe, ndipo tidye, tisekere;

24. cifukwa mwana wanga uyu anali wakufa, ndipo akhalanso wamoyo; anali wotayika, ndipo wapezedwa. Ndipo anayamba kusekera.

25. Koma mwana wace wamkuru anali kumunda. Ndipo pakubwera iye ndi kuyandikira kunyumba, anamva kuyimba ndi kubvina.

26. Ndipo anaitana mmodzi wa anayamata, namfunsa, Zinthu izi nzotani?

27. Ndipo uyu anati kwa iye, Mng'ono wako wafika; ndipo atate wako anapha mwana wa ng'ombe wonenepa, cifukwa anamlandira iye wamoyo.

28. Koma anakwiya, ndipo sanafuna kulowamo, Ndipo atate wace anaturuka namdandaulira.

29. Koma anayankha nati kwa atate wace, Onani, ine ndinakhala kapolo wanu zaka zambiri zotere, ndipo sindinalakwira lamulo lanu nthawi iri yonse; ndipo simunandipatsa ine kamodzi konse mwana wa mbuzi, kuti ndisekere ndi abwenzi anga.

Werengani mutu wathunthu Luka 15