Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 15:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma amisonkho onse ndi anthu ocimwa analikumyandikira kudzamva iye.

2. Ndipo Afarisi ndi alembi anadandaula nati, Uyu alandira anthu ocimwa, nadya nao.

3. Koma anati kwa iwo fanizo ili, nanena,

4. Munthu ndani wa inu ali nazo nkhosa makumikhumi, ndipo pakutayika imodzi ya izo, sasiya nanga m'cipululu zinazo makumi asanu ndi anai mphambu zisanu ndi zinai, nalondola yotayikayo kufikira aipeza?

5. Ndipo pamene adaipeza, aisenza pa mapewa ace wokondwera.

6. Ndipo pakufika kunyumba kwace amema abwenzi ace ndi anansi ace, nanena nao, Kondwerani ndi ine, cifukwa ndinapeza nkhosa yanga yotayikayo.

Werengani mutu wathunthu Luka 15