Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 13:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. ndipo, ngati udzabala cipatso kuyambira pamenepo, cabwino; koma ngati iai, mudzaulikhatu.

10. Ndipo analikuphunzitsa m'sungagoge mwina, tsiku la Sabata.

11. Ndipo mkazi anali nao mzimu wakumdwalitsa zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu; nakhala wopeteka, ndimo analibe mphamvu konse yakuweramuka.

12. Ndipo Yesu m'mene anamuona, anamuitana, nanena naye, Mkaziwe, wamasulidwa kudwala kwako.

13. Ndipo anaika manja ace pa iye; ndipo pomwepo anaongoledwa, nalemekeza Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Luka 13