Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 13:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo anati kwa wosungira munda wamphesa, Taona, zaka zapita zitatu ndimadza ine kudzafuna cipatso pa mkuyu uwu, ndipo ndimapeza palibe: taulikha; uyeseranjinso nthaka yopanda pace?

8. Ndipo iye anayankha nanena naye, Mbuye, baulekani ngakhale caka cino comwe, kufikira ndidzaukumbira kwete, ndithirepo ndowe;

9. ndipo, ngati udzabala cipatso kuyambira pamenepo, cabwino; koma ngati iai, mudzaulikhatu.

10. Ndipo analikuphunzitsa m'sungagoge mwina, tsiku la Sabata.

Werengani mutu wathunthu Luka 13