Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 13:28-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Kudzakhala komweko kulira ndi kukukuta mano, pamene mudzaona Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo, ndi aneneri onse, mu. Ufumu wa Mulungu, koma inu nokha muturutsidwa kunja.

29. Ndipo anthu adzacokera kum'mawa, ndi kumadzulo, ndi kumpoto, ndi kumwela, nadzakhalapansi mu Ufumu wa Mulungu.

30. Ndipo onani, alipo akuthungo amene adzakhala oyamba, ndipo alipo oyamba adzakhala akuthungo.

31. Nthawi yomweyo anadzapo Afarisi ena, nanena kwa iye, Turukani, cokani kuno; cifukwa Herode afuna kupha lou.

32. Ndipo iye anati kwa iwo, Pitani kauzeni nkhandweyo, Taonani, nditurutsa ziwanda, nditsiriza maciritso lero ndi mawa, ndipo mkuca nditsirizidwa.

33. Komatu ndiyenera ndipite ulendo wanga lero ndi mawa ndi mkuca, cifukwa sikuloleka kuti mneneri aonongeke kunja kwace kwa Yerusalemu.

34. Yerusalemu, Yerusalemu, iwe wakupha aneneri, ndi wakuponya miyala iwo atumidwa kwa iwe! ha! kawiri kawiri ndinafuna kusonkhanitsa ana ako, monga ngati thadzi ndi anapiye ace m'mapiko ace, ndipo simunafunai!

35. onani nyumba yanu isiyidwa kwa inu yabwinja; ndipo ndinena kwa inu kuti, Simudzandiona Ine, kufikira mudzati, Wolemekezeka iye amene akudza m'dzina la Ambuye.

Werengani mutu wathunthu Luka 13