Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 13:26-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. pomwepo mudzayambakunena, Ifetinadya ndi kumwa pamaso panu, ndipo munaphunzitsa m'makwalala a kwathu;

27. ndipo iye adzati, Ndinena kwa inu, sindidziwa kumene mucokera inu; cokani pa Ine, nonse akucita cosalungama,

28. Kudzakhala komweko kulira ndi kukukuta mano, pamene mudzaona Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo, ndi aneneri onse, mu. Ufumu wa Mulungu, koma inu nokha muturutsidwa kunja.

29. Ndipo anthu adzacokera kum'mawa, ndi kumadzulo, ndi kumpoto, ndi kumwela, nadzakhalapansi mu Ufumu wa Mulungu.

30. Ndipo onani, alipo akuthungo amene adzakhala oyamba, ndipo alipo oyamba adzakhala akuthungo.

Werengani mutu wathunthu Luka 13