Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 13:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo pamene Iye anatero, onse aja akutsutsana naye ananyazitsidwa; ndipo anthu onse a m'khamu anakondwera ndi zinthu zonse za ulemererozo zinacitidwa ndi iye.

18. Pamenepo ananena, Ufumu wa Mulungu ufanana ndi ciani? ndipo ndidzaufanizira ndi ciani?

19. Ufanana ndi kambeu kampiru, kamene munthu anatenga, nakaponya m'munda wace wace, ndipo kanamera, kanakula mtengo; ndi mbalame za m'mlengalenga zinabindikira mu nthambi zace.

20. Ndiponso anati, Ndidzafanizira Ufumu wa Mulungu ndi ciani?

21. Ufanana ndi cotupitsa mikate, cimene mkazianatenga, nacibisa mu miyeso itatu ya ufa, kufikira unatupa wonsewo,

22. Ndipo Iye anapita pakati pa mizinda ndi midzi, naphunzitsa, nayenda ulendo kunkabe ku Yerusalemu.

Werengani mutu wathunthu Luka 13