Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 13:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anakhalako nthawi yomweyo, anthu ena amene anamuuza iye za Agalileya, amene Pilato anasanganiza mwazi wao ndi nsembe zao.

2. Ndipo iye anayankha nati kwa iwo, Kodi muyesa kuti Agalileya aja anali anthu akucimwa koposa Agalileya onse, cifukwa anamva zowawa izi?

3. Ndinena kwa inu, iaitu; koma ngati inu simutembenuka mtima, mudzaonongeka nonse momwemo.

4. Kapena iwo aja khumi ndi asanu ndi atatu, amene nsanja yaitali ya m'Siloamu inawagwera, ndi kuwapha; kodi muyesa kuti iwo anali olakwa koposa anthu onse akukhala m'Yerusalemu?

5. Ndinena kwa inu, Iaitu; koma ngati simutembenuka mtima, mudzaonongeka nonse ci, modzimodzi.

Werengani mutu wathunthu Luka 13