Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 11:41-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. koma patsani mphatso yacifundo za m'katimo; ndipo onani, zonse ziri zoyera kwa inu.

42. Koma tsoka inu, Afarisi! cifukwa mupereka limodzi la magawo khumi la timbeu tonunkhira, ndi timbeu tokometsa cakudya ndi ndiwo zonse, ndipo mumaleka ciweruziro ndi cikondi ca Mulungu; mwenzi mutacita izi, ndi kusasiya zinazo.

43. Tsoka inu, Afarisi! cifukwa mukonda mipando yaulemu m'masunagoge, ndi kulankhulidwa m'misika.

44. Tsoka inu! cifukwa muli ngati manda osaoneka, ndipo anthu akuyendayenda pamwamba pao sadziwa,

Werengani mutu wathunthu Luka 11