Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 11:2-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo anati kwa iwo, M'mene mupemphera nenani, Atate, Dzina lanu liyeretsedwe; Ufumu wanu udze;

3. tipatseni ife tsiku ndi tsiku cakudya ca patsiku.

4. Ndipo mutikhululukire ife macimo athu; pakuti ifenso tikhululukira munthu yense wa mangawa athu. Ndipo musatitengere ife kokatiyesa.

5. Ndipo anati kwa iwo, Ndani wa inu adzakhala ndi bwenzi lace, nadzapita kwa iye pakati pa usiku, nadzati kwa iye, Bwenzi, ndibwereke mikate itatu;

6. popeza wandidzera bwenzi langa locokera paulendo, ndipo ndiribe compatsa;

7. ndipo iyeyu wa m'katimo poyankha akati, Usandibvuta; pakhomo mpotseka tsopano, ndipo ana anga ali nane pamodzi pogona; sindikhoza kuuka ndi kukupatsa?

8. Ndinena ndi inu, ngakhale sadzauka ndi kumpatsa, cifukwa ali bwenzi lacevkoma cifukwa ca liuma lace adzauka nadzampatsa iye ziri zonse azisowa.

9. Ndipo Ine ndinena ndi inu, Pemphani, ndipo adzakupatsani; funani, ndipo mudzapeza; gogodani ndipo adzakutsegulirani.

10. Pakuti yense wakupempha alandira; ndi wofunayo apeza; ndi iye amene agogoda adzamtsegulira.

11. Ndipo ndani wa inu ali atate, mwana wace akadzampempha mkate, adzampatsa mwala? kapena nsomba, nadzamninkha njoka m'malo mwa nsomba?

12. kapena akadzampempha dzira kodi adzampatsa cinkhanira?

Werengani mutu wathunthu Luka 11