Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 11:15-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Koma ena mwa iwo anati, Ndi Beelzebule mkuru wa ziwanda amaturutsa ziwanda.

16. Koma ena anamuyesa, nafuna kwa iye cizindikilo cocokera Kumwamba.

17. Koma iye, podziwa zolingirira zao, anati kwa iwo, Ufumu uli wonse wogawanika m'kati mwace upasuka; ndipo nyumba ikagawanika m'kati mwace igwa.

18. Ndiponso ngati Satana agawanika kudzitsutsa mwini, udzaimika bwanji ufumu wace? popeza munena kuti nditurutsa ziwanda ndi Beelzebule.

19. Koma ngati Ine ndimaturutsa ziwanda ndi Beelzebule, ana anu aziturutsa ndi yani? Mwa ici iwo adzakhala oweruza anu.

20. Koma ngati Ine nditurutsa ziwanda ndi cala ca Mulungu, pamenepo Ufumu wa Mulungu wafikira inu.

21. Pamene pali ponse mwini mphamvu alonda pabwalo pace zinthu zace ziri mumtendere;

22. koma pamene pali ponse amdzera wakumposa mphamvu, nakamlaka, amcotsera zida zace zonse zimene anazitama, nagawa zofunkha zace.

23. Iye wosabvomerezana ndi Ine atsutsana ndi Ine; ndipo iye wosasonkhanitsa pamodzi ndi Ine amwaza.

Werengani mutu wathunthu Luka 11