Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 11:14-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo analikuturutsa ciwanda cosalankhula. Ndipo kunali, citaturuka ciwanda, wosalankhulayo analankhula; ndipo makamu a anthu anazizwa.

15. Koma ena mwa iwo anati, Ndi Beelzebule mkuru wa ziwanda amaturutsa ziwanda.

16. Koma ena anamuyesa, nafuna kwa iye cizindikilo cocokera Kumwamba.

17. Koma iye, podziwa zolingirira zao, anati kwa iwo, Ufumu uli wonse wogawanika m'kati mwace upasuka; ndipo nyumba ikagawanika m'kati mwace igwa.

18. Ndiponso ngati Satana agawanika kudzitsutsa mwini, udzaimika bwanji ufumu wace? popeza munena kuti nditurutsa ziwanda ndi Beelzebule.

19. Koma ngati Ine ndimaturutsa ziwanda ndi Beelzebule, ana anu aziturutsa ndi yani? Mwa ici iwo adzakhala oweruza anu.

20. Koma ngati Ine nditurutsa ziwanda ndi cala ca Mulungu, pamenepo Ufumu wa Mulungu wafikira inu.

Werengani mutu wathunthu Luka 11