Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 10:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo m'nyumba iri yonse mukalowamo muthange mwanena, Mtendere ukhale pa nyumba iyi.

6. Ndipo mukakhala mwana wa mtendere m'menemo, mtendere wanu udzapumula pa iye; koma ngati mulibe, udzabwerera kwa inu.

7. Ndipo m'nyumba momwemo khalani, ndi kudya ndi kumwa za kwao; pakuti wanchito ayenera mphotho yace; musacokacoka m'nyumba.

8. Ndipo m'mudzi uli wonse mukalowamo, ndipo alandira inu, idyani zomwezi akupatsani;

Werengani mutu wathunthu Luka 10