Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 10:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mukani; taonani, Ine ndituma inu ngati ana a nkhosa pakati pa mimbulu.

4. Musanyamule thumba la ndalama kapena thumba la kamba, kapena nsapato; nimusalankhule munthu panjira.

5. Ndipo m'nyumba iri yonse mukalowamo muthange mwanena, Mtendere ukhale pa nyumba iyi.

6. Ndipo mukakhala mwana wa mtendere m'menemo, mtendere wanu udzapumula pa iye; koma ngati mulibe, udzabwerera kwa inu.

7. Ndipo m'nyumba momwemo khalani, ndi kudya ndi kumwa za kwao; pakuti wanchito ayenera mphotho yace; musacokacoka m'nyumba.

Werengani mutu wathunthu Luka 10