Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 10:3-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mukani; taonani, Ine ndituma inu ngati ana a nkhosa pakati pa mimbulu.

4. Musanyamule thumba la ndalama kapena thumba la kamba, kapena nsapato; nimusalankhule munthu panjira.

5. Ndipo m'nyumba iri yonse mukalowamo muthange mwanena, Mtendere ukhale pa nyumba iyi.

6. Ndipo mukakhala mwana wa mtendere m'menemo, mtendere wanu udzapumula pa iye; koma ngati mulibe, udzabwerera kwa inu.

7. Ndipo m'nyumba momwemo khalani, ndi kudya ndi kumwa za kwao; pakuti wanchito ayenera mphotho yace; musacokacoka m'nyumba.

8. Ndipo m'mudzi uli wonse mukalowamo, ndipo alandira inu, idyani zomwezi akupatsani;

9. ndipo ciritsani odwala ali mamwemonimunene nao, Ufumu wa Mulungu wayandikira kwa inu. Koma ku mudzi uli wonse mukalowako,

10. ndipo salandira inu, m'mene mwaturuka ku makwalala ace nenani,

Werengani mutu wathunthu Luka 10