Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 10:22-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Zonse zaperekedwa kwa Ine ndi Atate wanga; ndipo palibe munthu azindikira Mwana ali yani, koma Atate; ndipo Atate ali yani, koma Mwana, ndi iye amene Mwana afuna kumuululira iye.

23. Ndipo m'mene anapotolokera kwa ophunzira ace, ali pa okha, anati, Odala masowo akuona zimene muona.

24. Pakuti ndinena ndi inu kuti 1 aneneri ndi mafumu ambiri anafuna kuona zimene inu muziona, koma sanaziona; ndi kumva zimene mukumva, koma sanazimva.

25. Ndipo taonani, wacilamulo wina anaimirira namuyesa iye, nanena, 2 Mphunzitsi, ndidzalowa moyo wosatha ndi kucita ciani?

26. Ndipo anati kwa iye, M'cilamulo mulembedwa ciani? Uwerenga bwanji?

27. Ndipo iye anayankha nati, 3 Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu yako yonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mnansi wako monga iwe mwini.

28. Ndipo anati kwa iye, Wayankha bwino; cita ici, ndipo udzakhala ndi moyo.

Werengani mutu wathunthu Luka 10