Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 10:16-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. iye wakumvera inu, andimvera Ine; ndipo iye wakukana inu, andikana Ine; ndipo iye wakukana Ine amkana iye amene anandituma Ine.

17. Ndipo makumi asanu ndi awiri aja anabwera mokondwera, nanena, Ambuye, zingakhale ziwanda zinatigonjera ife m'dzina lanu.

18. Ndipo anati kwa iwo, Ndinaona Satana alinkugwa ngati mphezi wocokera kumwamba.

19. Taonani, ndakupatsani ulamuliro wakuponda pa njoka ndi zinkhanira, ndi pa mphamvu iri yonse ya mdaniyo; ndipo kulibe kanthu kadzakuipsani konse.

20. Koma musakondwera nako kuti mizimu idakugonjerani, koma kondwerani kuti maina anu alembedwa m'Mwamba.

21. Nthawi yomweyo iye anakondwera ndi Mzimu Wovera, nati, Ndikubvomerezani Inu, Atate, Ambuye wa kumwamba ndi wa dziko, kuti izi munazibisira anzeru ndi ozindikira, ndipo munaziululira ana amakanda; indedi, Atate, pakuti kotero kudakondweretsa pamaso panu.

22. Zonse zaperekedwa kwa Ine ndi Atate wanga; ndipo palibe munthu azindikira Mwana ali yani, koma Atate; ndipo Atate ali yani, koma Mwana, ndi iye amene Mwana afuna kumuululira iye.

23. Ndipo m'mene anapotolokera kwa ophunzira ace, ali pa okha, anati, Odala masowo akuona zimene muona.

24. Pakuti ndinena ndi inu kuti 1 aneneri ndi mafumu ambiri anafuna kuona zimene inu muziona, koma sanaziona; ndi kumva zimene mukumva, koma sanazimva.

25. Ndipo taonani, wacilamulo wina anaimirira namuyesa iye, nanena, 2 Mphunzitsi, ndidzalowa moyo wosatha ndi kucita ciani?

26. Ndipo anati kwa iye, M'cilamulo mulembedwa ciani? Uwerenga bwanji?

27. Ndipo iye anayankha nati, 3 Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu yako yonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mnansi wako monga iwe mwini.

28. Ndipo anati kwa iye, Wayankha bwino; cita ici, ndipo udzakhala ndi moyo.

Werengani mutu wathunthu Luka 10