Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 1:6-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo onse awiri anali olungama mtima pamaso pa Mulungu, namayendabe m'malamulo onse ndi zoikika za Ambuye osacimwa.

7. Ndipo analibe mwana, popeza Elisabeti anali wouma, ndipo onse awiri anakalamba.

8. Ndipo panali, pakucita iye nchito yakupereka nsembe m'dongosolo la gulu lace, pamaso pa Mulungu, monga mwa macitidwe a kupereka nsembe,

9. adamgwera maere akufukiza zonunkhira polowa iye m'Kacisi wa Ambuye.

10. Ndipo khamu lonse la anthu Iinalikupemphera kunja nthawi ya zonunkhira.

11. Ndipo anamuonekera iye mngelo wa Ambuye, naimirira ku dzanja lamanja la guwa la nsembe la zonunkhira.

12. Ndipo Zakariya anadabwa pamene anamuona, ndipo mantha anamgwira.

13. Koma mngelo anati kwa iye, Usaope Zakariya, cifukwa kuti lamveka pemphero lako, ndipo mkazi wako adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamucha dzina lace Yohane.

Werengani mutu wathunthu Luka 1