Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 9:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndi miliri iyi linaphedwa limodzi la magawo atatu a anthu, ndi moto, ndi utsi, ndi sulfure, zoturuka m'kamwa mwao.

19. Pakuti mphamvu ya akavalo in m'kamwa mwao, ndi m'micira yao; pakuti micira yao ifanana ndi njoka, nikhala nayo mitu, ndipo aipsa nayoyo.

20. Ndipo otsala a anthu osaphedwa nayo miliri iyo sanalapa nchito ya manja ao, kuti asapembedzere ziwanda, ndi mafano agolidi, ndi asiliva, ndi amkuwa, ndi amwala, ndi amtengo, amene sakhoza kupenya, kapena kumva, kapena kuyenda;

21. ndipo sanalapa mbanda zao, kapena nyanga zao, kapena cigololo cao, kapena umbala wao.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 9