Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 9:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo ciwerengero ca nkhondo za apakavalo ndico zikwi makumi awiri zocurukitsa zikwi khumi; ndinamva ciwerengero cao.

17. Ndipo kotero ndinaona akavalo m'masomphenya, ndi iwo akuwakwera akukhala nazo zikopa za moto, ndi huakinto ndi sulfure; ndi mitu ya akavalo ngati mitu ya mikango; ndipo m'kamwa mwao muturuka moto ndi utsi ndi sulfure.

18. Ndi miliri iyi linaphedwa limodzi la magawo atatu a anthu, ndi moto, ndi utsi, ndi sulfure, zoturuka m'kamwa mwao.

19. Pakuti mphamvu ya akavalo in m'kamwa mwao, ndi m'micira yao; pakuti micira yao ifanana ndi njoka, nikhala nayo mitu, ndipo aipsa nayoyo.

20. Ndipo otsala a anthu osaphedwa nayo miliri iyo sanalapa nchito ya manja ao, kuti asapembedzere ziwanda, ndi mafano agolidi, ndi asiliva, ndi amkuwa, ndi amwala, ndi amtengo, amene sakhoza kupenya, kapena kumva, kapena kuyenda;

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 9