Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 3:10-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Popeza unasunga mau a cipiriro canga, Inenso ndidzakusunga kukulanditsa mu nthawi ya kuyesedwa, ikudza pa dziko lonse lapansi, kudzayesa iwo akukhala padziko.

11. Ndidza msanga; gwira cimene uli naco, kuti wina angalande korona wako.

12. Iye wakulakika, ndidzamyesa iye mzati wa m'Kacisi wa Mulungu wanga, ndipo kuturuka sadzaturukamonso; ndipo ndidzalemba pa iye dzina la Mulungu wanga, ndi dzina la mzinda wa Mulungu wanga, la Yerusalemu watsopano, wotsika m'Mwamba, kucokera kwa Mulungu wanga; ndi dzina langa latsopano.

13. Iye wakukhala nalo khutu amve cimene Mzimu anena kwa Mipingo.

14. Ndipo kwa mngelo wa Mpingo wa ku Laodikaya lemba:Izi anena Amenyo, mboni yokhulupirika ndi yoona, woyamba wa cilengo ca Mulungu:

15. Ndidziwa nchito zako, kuti suli wozizira kapena wotentha: mwenzi utakhala wozizira kapena wotentha.

16. Kotero, popeza uti wofunda, wosati wotentha kapena wozizira, ndidzakulabvula m'kamwa mwanga.

17. Cifukwa unena kuti ine ndine wolemera, ndipo cuma ndiri naco, osasowa kanthu; ndipo sudziwa kuti ndiwe watsoka, ndi wocititsa cifundo, ndi wosauka, ndi wakhungu, ndi wausiwa;

18. ndikulangiza ugule kwa Ine golidi woyengeka m'moto, kuti ukakhale wacuma, ndi zobvala zoyera, kuti ukadzibveke, ndi kuti manyazi a usiwa wako asaoneke; ndi mankhwala opaka m'maso mwako, kuti ukaone.

19. Onse amene ndiwakonda, ndiwadzudzula ndi kuwalanga; potero cita cangu, nutembenuke mtima.

20. Taona, ndaima pakhomo, ndigogoda; wina akamva mau anga nakatsegula pakhomo, ndidzalowa kwa iye, ndipo ndidzadya naye, ndi iye ndi Ine.

21. Iye wakulakika, ndidzampatsa akhale pansi ndi Ine pa mpando wacifumu wanga, monga Inenso ndinalakika, ndipo ndinakhala pansi ndi Atate wanga pa mpando wacifumu wace.

22. Iye wakukhala nalo khutu amve cimene Mzimu anena kwa Mipingo.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 3