Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 22:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndicita umboni kwa munthu ali yense wakumva mau a cinenero ca buku ili, 1 Munthu akaonjeza pa awa, adzamuonjezera Mulungu miliri yolembedwa m'bukumu:

19. ndipo 2 ali yense akacotsako pa mau a buku la cinenero ici, Mulungu adzamcotsera gawo lace pa mtengo wa moyo, ndi 3 m'mzinda woyerawo, ndi pa izi zilembedwa m'bukumu.

20. Iye wakucitira umboni izi, anena, 4 Indetu; ndidza msanga. Amen; idzani, Ambuye Yesu.

21. 5 Cisomo ca Ambuye Yesu cikhale ndi oyera mtima onse, Amen.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 22