Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 2:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Komatu ndiri nazo zinthu pang'ono zotsutsana ndi iwe, popeza uli nao komweko akugwira ciphunzitso ca Balamu, amene anaphunzitsa Balaki aponye cokhumudwitsa pamaso pa ana a Israyeli, kuti adye zoperekedwa nsembe kwa mafano, nacite cigololo.

15. Kotero uli nao akugwira ciphunzitso ca Anikolai momwemonso.

16. Cifukwa cace lapa; ukapanda kutero ndidza kwa iwe posacedwa, ndipo ndidzacita nao nkhondo ndi lupanga la m'kamwa mwanga.

17. Iye wakukhala nalo khutu amve cimene Mzimu anena kwa Mipingo. Kwa iye wolakika, ndidzampatsa mana obisika, ndipo ndidzampatsa mwala woyera, ndi pa mwalawo dzina latsopano lolembedwapo, wosalidziwa munthu ali yense koma iye wakuulandira.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 2