Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 18:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Zitatha izi ndinaona mngelo wina wakutsika m'Mwamba wakukhala nao ulamuliro waukuru; ndipo dziko linaunikidwa ndi ulemerero wace.

2. Ndipo anapfuula ndi mau olimba, nanena, Wagwa, wagwa, Babulo waukuru, nusandulika mokhalamo ziwanda, ndi mosungiramo mizimu yonse yonyansa, ndi mosungiramo mbalame zonse zonyansa ndi zodanidwa.

3. Cifukwa ndi vinyo wa mkwiyo wa cigololo cace mitundu yonse idagwa; ndipo mafumu a dziko anacita naye cigololo; ndipo ocita malonda a dziko analemera ndi mphamvu ya kudyererakwace.

4. Ndipo ndinamva mau ena ocokera Kumwamba, nanena, Turukani m'menemo, anthu anga; kuti mungayanjane ndi macimo ace, ndi kuti mungalandireko ya miliri yace;

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 18