Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 17:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anadza mmodzi mwa angelo asanu ndi awiri akukhala nazo mbale zisanu ndi ziwiri, nalankhula ndi ine, nanena, Idza kuno, ndidzakuonetsa citsutso ca mkazi wacigololo wamkuru, wakukhala pa madzi ambiri,

2. amene mafumu a dziko anacita cigololo naye, ndipo iwo akukhala padziko analedzera ndi vinyo wa cigololo cace.

3. Ndipo ananditenga kumka nane kucipululu, mu Mzimu; ndipo ndinaona mkazi alinkukhala pacirombo cofiiritsa, codzala ndi maina a mwano, cakukhala nayo mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 17