Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 16:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. (Taonani, ndidza ngati mbala. Wodala iye amene adikira, nasunga zobvala zace, kuti angayende wausiwa, nangapenye anthu usiwa wace.)

16. Ndipo anawasonkhanitsira ku malo ochedwa m'Cihebri Harmagedo.

17. Ndipo wacisanu ndi ciwiri anatsanulira mbale yace mumlengalenga; ndipo m'Kacisimo mudaturuka mau akuru, ocokera ku mpando wacifumu ndi kunena, Cacitika;

18. ndipo panakhala mphezi, ndi mau, ndi mabingu; ndipo panali 1 cibvomezi cacikuru cotero sicinaoneke ciyambire anthu padziko, cibvomezi colimba cotero, cacikuru cotero.

19. Ndipo 2 cimudzi cacikuruco cidagawika patatu, ndi midzi ya amitundu inagwa; ndipo 3 Babulo waukuru unakumbukika pamaso pa Mulungu, kuti aupatse cikho ca vinyo wamkali wa mkwiyo wace.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 16