Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 14:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo mngelo wina anaturuka m'Kacisi ali m'Mwamba, nakhala nalo zenga lakuthwa nayenso.

18. Ndipo mngelo wina anaturuka pa guwa la nsembe, ndiye wakukhala nao ulamuliro pamoto; napfuula ndi mau akuru kwa iye wakukhala nalo zenga lakuthwa, nanena, 1 Tumiza zenga lako lakuthwa, nudule matsango a munda wampesa wa m'dziko; pakuti mphesa zace zapsa ndithu.

19. Ndipo mngelo anaponya zenga lace ku dziko nadula mphesa za m'munda wa m'dziko, 2 naziponya moponderamo mphesa mwamukuru mwa mkwiyo wa Mulungu.

20. Ndipo 3 moponderamo mphesa anamuponda kunja kwa mudzi, ndipo mudaturuka mwazi moponderamo mphesa, kufikira zapakamwa za akavalo, kufikira mastadiya cikwi ndi mazana asanu ndi limodzi.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 14