Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 1:17-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo pamene ndinamuona iye, ndinagwa pa mapazi ace ngati wakufa; ndipo anaika dzanja lace lamanja pa ine, nati, Usaope, ine ndine woyamba ndi wotsiriza,

18. ndi Wamoyoyo; ndipo 1 ndinali wakufa, ndipo taona, ndiri wamoyo kufikira nthawi za nthawi, ndipo ndiri nazo zofungulira za imfa ndi Hade.

19. Cifukwa cace 2 lembera zimene unaziona, ndi zimene ziripo, ndi zimene zidzaoneka m'tsogolomo;

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 1