Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 1:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. CIBVUMBULUTSO ca Yesu Kristu, cimene Mulungu anambvumbulutsira acionetsere akapolo ace, ndico ca izi ziyenera kucitika posacedwa: ndipo potuma mwa mngelo wace anazindikiritsa izi kwa kapolo wace Yohane;

2. amene anacita umboni za mau a Mulungu, ndi za umboni wa Yesu Kristu, zonse zimene adaziona.

3. Wodala iye amene awerenga, ndi iwo amene akumva mau a cineneroco, nasunga zolembedwa momwemo; pakuti nthawi yayandikira.

4. Yohane kwa Mipingo isanu ndi wiri m'Asiya: Cisomo kwa inu ndi ntendere, zocokerakwa iye amene ili, ndi amene adali, ndi amene aliikudza; ndi kwa mizimu isanu ndi wiri yokhala ku mpando wacifumu vace;

5. ndi kwa Yesu Kristu, mboli yokhulupirikayo, wobadwa woyanba wa akufa, ndi mkulu wa mafunu a dziko lapansi, Kwa iye ameieatikonda ife, natimasula ku macimo athu ndi mwazi wace;

6. natiyesa ife ufumu tikhale ansembe a Mulungu ndiye Atate wace; kwa iye kukhale ulemerero ndi mphamvu kufikira nthawi za nthawi. Amen.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 1