Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 6:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. ndipo pamene munamasulidwa kuucimo, munakhala akapolo a cilungamo,

19. Ndilankhula manenedwe a anthu, cifukwa ca kufoka kwa thupi lanu; pakuti monga inu munapereka ziwalo zanu zikhale akapolo a conyansa ndi a kusayeruzika kuti zicite kusayeruzika, inde kotero tsopano perekani ziwalo zanu zikhale akapolo a cilungamo kuti zicite ciyeretso.

20. Pakuti pamene inu munali aka polo a ucimo, munali osatumikira cilungamo.

21. Ndipo munali nazo zobala zanji nthawi ija, m'zinthu zimene mucita nazo manyazi tsopano? pakuti cimariziro ca zinthu izi ciri imfa.

22. Koma tsopano, pamene munamasulidwa kuucimo, ndi kukhala akapolo a Mulungu, muli naco cobala canu cakufikira ciyeretso, ndi cimariziro cace moyo wosatha.

23. Pakuti mphotho yace ya ucimo ndi imfa; koma mphatso yaulere ya Mulungu ndiyo moyo wosatha wa mwa Kristu Yesu Ambuye wathu.

Werengani mutu wathunthu Aroma 6