Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 16:2-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. kuti mumlandire iye mwa Ambuye, monga kuyenera oyera mtima, ndi kuti mumthandize m'zinthu zili zonse adzazifuna kwa inu; pakuti iye yekha anali wosungira ambiri, ndi ine ndemwe.

3. Mulankhule Priska ndi Akula, anchito anzanga m'Kristu Yesu,

4. amene anapereka khosi lao cifukwa ca moyo wanga; amene ndiwayamika, si ine ndekha, komanso Mipingo yonse ya Ambuye ya kwa anthu amitundu;

5. ndipo mulankhule Mpingo wa Ambuye wa m'nyumba mwao. Mulankhule Epeneto wokondedwa wanga, ndiye cipatso coundukula ca Asiya ca kwa Kristu,

6. Mulankhule Mariya amene anadzilemetsa ndi nchito zambiri zothandiza inu.

7. Mulankhule Androniko ndi Yuniya, anansi anga, ndi andende anzanga, amene ali omveka mwa amitumwi, amenenso ananditsogolera ine mwa Kristu.

8. Mulankhule Ampliato wokondedwa wanga mwa Ambuye.

9. Mulankhule Urbano wanchito mnzathu mwa Kristu, ndi Staku wokondedwa wanga,

10. Mulankhule Apele, wobvomerezedwayo mwa Kristu, Mulankhule iwo a kwa Aristobulo.

11. Mulankhule Herodiona, mbale wanga. Mulankhule iwo a kwa Narkiso, amene ali mwa Ambuye.

12. Mulankhule Trufena, ndi Trufosa amene agwiritsa nchito mwa Ambuyeo Mulankhule. Persida, wokondedwayo amene anagwiritsa nchito zambiri mwa Ambuye.

Werengani mutu wathunthu Aroma 16