Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 14:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Usapasule nchito ya Mulungu cifukwa ca cakudya. Zinthu zonse ziri zoyera; koma kuli koipa kwa munthu amene akudya ndi kukhumudwa.

21. Kuli kwabwino kusadya nyama, kapena kusamwa vinyo, kapena kusacita cinthu ciri conse cakukhumudwitsa mbale wako.

22. Cikhulupiriro cimene uli naco, ukhale naco kwa iwe wekha pamaso pa Mulungu. Wodala ndiye amene sadziweruza mwini yekha m'zinthu zomwe iye wazibvomereza.

23. Koma iye amene akayika-kayika pakudya, atsutsika, cifukwa akudya wopanda cikhulupiriro; ndipo cinthu ciri conse cosaturuka m'cikhulupiriro, ndico ucimo.

Werengani mutu wathunthu Aroma 14