Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 14:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Pakuti iye amene atumikira Kristu mu izi akondweretsa Mulungu, nabvomerezeka ndi anthu.

19. Cifukwa cace tilondole zinthu za mtendere, ndi zinthu zakulimbikitsana wina ndi mnzace.

20. Usapasule nchito ya Mulungu cifukwa ca cakudya. Zinthu zonse ziri zoyera; koma kuli koipa kwa munthu amene akudya ndi kukhumudwa.

21. Kuli kwabwino kusadya nyama, kapena kusamwa vinyo, kapena kusacita cinthu ciri conse cakukhumudwitsa mbale wako.

Werengani mutu wathunthu Aroma 14