Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 11:20-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Cabwino; iwo anathyoledwa ndi kusakhulupirira kwao, ndipo iwe umaima ndi cikhulupiriro cako. Usamadzikuza mumtima, koma opatu:

21. pakuti ngati Mulungu sanaleka nthambi za mtundu wace, inde sadzakuleka iwe.

22. Cifukwa cace onani cifatso ndi kuuma mtima kwace kwa Mulungu: kwa iwo adagwa, kuuma kwace; koma kwa iwe cifatso cace ca Mulungu, ngati ukhala cikhalire m'eifatsomo; koma ngati sutero, adzakusadza iwe.

23. Ndipo iwonso, ngati sakhala cikhalire ndi cisakhulupiriro, adzawamezanitsanso.

24. Pakuti ngati iwe unasadzidwa ku mtengo wazitona wa mtundu wa kuthengo, ndipo unamezetsanidwa ndi mtengo wazitona wabwino, mokaniza makhalidwe ako; koposa kotani nanga iwo, ndiwo nthambi za mtundu wace, adzamezetsanidwa ndi mtengo wao womwewo wazitona?

25. Pakuti sindifuna, abale, kuti mukhale osadziwa cinsinsi ici, kuti mungadziyese anzeru mwa inu nokha, kuti kuuma mtima kunadza pang'ono pa Israyeli, kufikira kudzaza kwa anthu amitundu kunalowa;

26. ndipo cotero Israyeli yense adzapulumuka; monganso kunalembedwa, kuti,Adzaturuka ku Ziyoni Mpulumutsi;Iye adzacotsa zamwano kwa Yakobo:

27. Ndipo ici ndi cipangano canga ndi iwo,Pamene ndidzacotsa macimo ao.

28. Kunena za Uthenga Wabwino, iwo ali ngati adani, cifukwa ca inu; koma kunena za cisankhidwe, z ali okondedwa, cifukwa ca makolo.

29. Pakuti 1 mphatso zace ndi kuitana kwace kwa Mulungu sizilapika.

30. Pakuti 2 monga inunso kale simunamvera Mulungu, koma tsopano mwalandira cifundo mwa kusamvera kwao,

31. coteronso iwo sanamvera tsopano, kuti iwonso akalandire cifundo, cifukwa ca cifundo ca kwa inu.

32. Pakuti 3 Mulungu anatsekera pamodzi onse m'kusamvera, kuti akacitire onse cifundo.

33. Ha! kuya kwace kwa kulemera ndi kwa nzeru ndi kwa kudziwa kwace kwa Mulungu! 4 Osasanthulikadi maweruzo ace, ndi njira zace nzosalondoleka!

34. Pakuti 5 anadziwitsa ndani mtima wace wa Ambuye? Kapena anakhala mphungu wace ndani?

Werengani mutu wathunthu Aroma 11