Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 10:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo iwo adzaitana bwanji pa iye amene sanamkhulupirira? ndipo adzakhulupirira bwanji iye amene sanamva za iye? ndipo adzamva bwanji wopanda wolalikira?

15. ndipo adzalalikira bwanji, ngati satumidwa? monganso kwalembedwa, Okometsetsa ndithu ali mapazi a iwo akulalikira Uthenga Wabwino wa zinthu zabwino.

16. Koma sanamvera Uthenga Wabwino onsewo. Pakuti Yesaya anena, Ambuye, anakhulupirira ndani zonena ife?

17. Comweco cikhulupiriro cidza ndi mbiri, ndi mbiri idza mwa mau a Kristu.

Werengani mutu wathunthu Aroma 10