Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aroma 1:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. cifukwa kuti, ngakhale anadziwa Mulungu, sanamcitira ulemu wakuyenera Mulungu, ndipo sanamyamika; koma anakhala opanda pace m'maganizo ao, ndipo unada mtima wao wopulukira,

22. Pakunena kuti ali anzeru, anapusa;

23. nasandutsa ulemerero wa Mulungu wosaonongeka, naufanizitsa ndi cifaniziro ca munthu woonongeka ndi ca mbalame, ndi ca nyama zoyendayenda, ndi ca zokwawa.

24. Cifukwa cace Mulungu anawapereka iwo m'zilakolako za mitima yao, kuzonyansa, kucititsana matupi ao wina ndi mnzace zamanyazi;

Werengani mutu wathunthu Aroma 1